29/08/2025
Bambo Poya akhala MP wathu kuyambira mu 2019, koma utsogoleri wake sunabweretse chitukuko chenicheni ku Zomba Ntonya. Mโmalo mopanga kuti anthu apindule ndi AIP (Affordable Input Programme), iye anangokhala busy kuthandiza atolankhani pomwe anthu ake ankavutika ndi njala komanso kusowa njira zothetsera kusowa chakudya.
Pamene njala inali pachimake, Masanga ndiye anaimira ndi anthu ake. Iye anagawa ma tonne oposa 60 a chimanga, kuti anthu apeze mpumulo. Komanso, Masanga wapereka mavaucha, omwe akupatsa anthu chiyembekezo kuti vuto la njala litha. Ndi mavauchawa, anthu adzatha kugula feteleza, kulima, komanso kupeza chimanga nthawi ya njala.
Chifukwa chokhacho chimene Masanga sali kugawa chimanga panopa ndi chakuti boma laletsa kugawa zakudya nthawi ya kampeni. Izi zikuwonetsa kulemekeza kwake malamulo, mosiyana ndi Poya yemwe ntchito yake ndi kuwononga ndondomeko za Masanga osati kuthandiza anthu.
Pa 16 September, tiyeni tipange chisankho cholondola. Tiyeni tichotse Bambo Poya amene watilephera, ndipo tisankhe Masanga, mtsogoleri amene ali ndi njira zenizeni zotithandiza kukhala odziyimira pawokha ku Zomba Ntonya.