14/03/2026
Pulezidenti Peter Mutharika wanena kuti iye ali kumbuyo kwa Komiti yoona zosankha anthu maudindo a boma ku parliament(PAC) yomwe ikufufuza pazakugulitsidwa kwa hotelo ya Amaryllis kupyolera mu ndalama zomwe zimasungidwa ndi bungwe loona za anthu ogwira ntchito m'boma.
Mutharika wati iye akutsatira nkhaniyi mwachidwi ndipo aonesesa kuti chilungamo chitsatidwe.
Komitiyi Khalapampando wake ndi Baba Steve Malondera.
Inuyo mukutipo bwanji? Kodi APM wabwera panthawi yake yomwe amafunika kutero kapena akanadikira kaye aone chitsogolo chake?