Miftaahul Jannah kiyi wa ku Jannah

Miftaahul Jannah kiyi wa ku Jannah Assalaam alaykum warahmatullahi wabarakaatuh
You are welcome to Mifaahul Jannah ou can share with us any massage with proof of Qur'aan and Hadeet saheeh

25/01/2021

41. (lye) adati: "Mbuye wanga! Ndipatseni Chizindikiro!" Adati: "Chizindikiro chako Ndikuti sudzatha kulankhula ndi anthu mpaka Masiku atatu koma momangolozera (ndi Chala) basi. Ndipo tamanda Mbuye wako, Kutamanda kwambiri ndiponso Umlemekeze (popemphera) madzulo Ndi m'mawa".

42. Ndipo (kumbukira) pamene angelo adati: "E Iwe Mariam! Ndithudi, Mulungu Wakusankha, Wakuyeretsa ndipo Wakulemekeza, mwa Akazi onse amitundu ya anthu".

🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
Apa patchulidwa nkhani ya mayi Mariam (Maria) pomwe adatha msinkhu ndi pomwe mngelo adamuuza nkhani yabwinoyi.

43. "E iwe Mariam, dzichepetse Kwa Mbuye wako ndi Kumlambira powerama pamodzi Ndi owerama".

44. Izi ndizina mwankhani zobisika zomwe Tikukuvumbulutsira. Sudali nawo pamene Amaponya zolembera zawo (m'madzi m'njira Ya mayere) kuti aone ndani mwaiwo alere Mariam. Sudali nawo pamene adali kutsutsana.

45. (Kumbukira) pamene mngelo adati: "E iwe Mariam (Maria)! Mulungu akukuuza nkhani Yabwino (kuti ubereka mwana popanda Mwamuna Koma kupyolera mu) liwu lochokera Kwa lye (Mulungu, lakuti, "Bereka," ndipo Nkubereka Popanda kupezana ndi mwamuna). Dzina lake ndi Mesiya Yesu mwana wa Mariya, adzakhala wolemekezeka padziko lapansi ndi pa Tsiku lachimaliziro; ndiponso ndi mmodzi wa Oyandikitsidwa kwa Mulungu.

46. "lye adzayankhula ndi anthu Ali mchikuta ndi kuukulu (Wake). Ndipo adzakhala Mmodzi wa anthu abwino".

47. (Mariam) adati: "Mbuye wanga! Ndingakhale ndi mwana Bwanji pomwe sadandikhudze Munthu aliyense (mwamuna)?" (Mngelo) adati: "Ndi Momwemo. Mulungu Amalenga chimene wafuna. Akafuna chinthu amachiuza: "Chitika," ndipo chimachitikadi.

48. Ndipo Mulungu adzamphunzitsa Kulemba, nzeru, Taurat ndi Injili.

49. "Ndipo (adzamchita kukhala) Mneneri Kwa ana a Israeli (adzakhala akuwauza kuti): "Ine ndakudzerani ndizizindikiro kuchokera Kwa Mbuye wanu kuti ndikuumbireni dongo Ngati chithunzi chambalame, nkuuzira M'menemo nkukhaladi mbalame Mwachilolezo cha Mulungu; Ndipo ndichiritsa osapenya chibadwire, Ndiwamangamaanga, ndi kuukitsa wakufa Mwa chilolezo cha Mulungu; ndipo ndikuuzani Zomwe mudye ndi zimene musunge m'nyumba Zanu.Ndithudi, m'zimenezi muli zizindikiro Kwa inu ngati mulidi anthu okhulupirira.

🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
Apa akunena zina mwazozizwitsa zomwe Mneneri Isa (Yesu) anadza nazo. Ndipo zina mwaizo ndikuumba ndidongo chifanizo chambalame. Kenako nkuchiuzira chikhaladi mbalame yamoyo mwachilolezo cha Mulungu.
°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°
50. "Ndipo (ndikhala) wotsimikizira zomwe Zidalipo patsogolo panga (m'Buku la) Taurat. Ndipo ndadza kuti ndikulolezeni Zina mwa zomwe zidaletsedwa kwa inu. Ndipo ndakudzerani ndi zizindikiro Kuchokera kwa Mbuye wanu (zotsimikizira Uthenga wanga). Choncho, opani Mulungu ndi kundimvera (ine).

51. "Ndithu Mulungu ndiye Mbuye wanga ndiponso Mbuye Wanu; choncho mupembedzeni. Iyi ndiyo njira yoongoka".

52. Koma pamene Yesu adazindikira mwa iwo Kusakhulupirira adati: "Ndani akhale athandizi Anga kwa Mulungu (popitiriza kufalitsa Chipembedzo Chake)?" Ophunzira ake Adati: "Ife ndife athandizi a Mulungu (pofalitsa Chipembedzo Chake). Takhulupirira Mulungu; ndipo ikira umboni kuti ife ndithu Ndi odzipereka (kwa Mulungu).

53. "Mbuye wathu! Tazikhulupirira Zimene mwavumbulutsa, Ndipo tamtsata Mtumikiyo. Choncho tilembeni pamodzi Ndi oikira umboniwo."

54. Ndipo (Ayuda) adakonza chiwembu (chofuna Kupha Yesu) Mulungu adachiwononga Chiwembu chawocho. Mulungu ngokhoza bwino zedi Poononga ziwembu za anthu a chiwembu.

55. (Kumbukirani) pamene Mulungu adati: "Iwe Yesu! Ine ndikukwaniritsira nyengo yako Yokhala ndi moyo. (Ayuda sachita kanthu Kwa iwe). Ndipo ndikunyamulira kwa Ine Ndikuyeretsa kwa anthu osakhulupirira (omwe Ndi adani ako). Ndipo amene akutsata (Iwe) Ndiwasankha kukhala apamwamba pa amene Sadakhulupirire kufikira tsiku lachimaliziro. Kenako kobwerera kwanu nkwa Ine, ndipo Ndidzaweruza pakati panu pazomwe mudali Kusiyana.

56. Tsono amene sadakhulupirire, Ndiwakhaulitsa ndi chilango chaukali padziko lapansi ndi tsiku lomaliza, ndipo Sadzapeza athandizi.

57. Koma amene akhulupirira Nachita zabwino, (Mulungu) adzawalipira malipiro Awo (mokwanira). Ndipo Mulungu Sakonda anthu ochita zoipa.

58. Izi tikukuwerengera iwezi Ndi zivumbulutso ndi ulaliki waluntha.

59. Ndithudi, fanizo la Yesu kwa Mulungu lili ngati fanizo la Adam; adamulenga ndi dothi namuuza kuti: "Khala munthu," Ndipo adakhaladi.

🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
(Ndime 59-62) Ndime iyi idavumbulutsidwa pamene nthumwi za chikhirisitu zidadza kwa mtumlki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) kuchokera ku Najirani. Iwowo adakangana ndi Mtumiki wa Mulungu pa nkhani ya Yesu. Iwo adati kwa Mtumiki wa Mulungu "Bwanji iwe ukutukwana Mneneri wathu?" lye adati: "Kodi ndikutukwana chotani?" Iwo adati: "Iwe ukuti iyeyo ndikapolo wa Mulungu." lye adati: "Inde. lyeyo ndi kapolo wa Mulungu ndiponso mawu ake omwe adawaponya mwanamwali." Zitatero iwo adapsa mtima ndipo anakwiya nati, "Kodi iwe udamuonapo munthu wobadwa popanda tate? Ngati ukunenadi zoona tationetsa munthu wotere." Apa mpomwe Mulungu adavumbulutsa ndime yakuti "Ndithudi, fanizo la Yesu (Isa) kwa Mulungu lili ngati fanizo la Adam". Kenako anawaitanira ku Chisilamu. Iwo adati: "Tidalowa kale m'Chisilamu iwe usanadze." Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adati: "Mwanama. Pali zinthu zitatu zikukuletsani kulowa m'Chisilamu: (a) Kunena kwanu mawu oti Mulungu wadzipangira mwana. (b) Kudya kwanu nyama ya nkhumba. (c) Kulambira kwanu mtanda." Pamene adapitiriza kumtsutsa Mneneri Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adawapempha kuti atembererane ponena kuti, "O! Ambuye Mulungu! Mtemberereni ndi kumlanga amene akunena zabodza mwaife pankhani ya Yesu! Pompo Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adasonkhanitsa anthu ake. Koma iwo atakhala upo adagwirizana kuti asalole kuopa kuti chilango chingawatsikire. Potero zidadziwika kwa anthu kuti iwo ngabodza.
°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°
60. (Ichi ndi) choona chochokera Kwa Mbuye wako; choncho Usakhale mwaokaikira.

23/01/2021

30. "Tsiku lomwe mzimu uliwonse Udzapeza zabwino zomwe Udachita zitabweretsedwa, Ndiponso zoipa zomwe udachita; Udzalakalaka kuti pakadakhala Mtunda wautali pakati Pamachimo ake ndi iye. Ndipo Mulungu Mwini Akukuchenjezani za chilango Chake. Ndipo Mulungu ngoleza Kwa akapolo ake. ¹

🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
¹ Tsiku lachimaliziro (kiyama) munthu adzalakalaka kuti asawaone machimo ake amene adachita. Koma kuti machimowo akhale kutali ndi iye pomwe machimowo akamawachita amakhala wosangalala.
°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°
31. Nena: (iwe Mtumiki) "Ngati inu Mukumkonda Mulungu, tsatani ine; Mulungu akukondani Ndikukukhululukirani machimo Anu. Ndipo Mulungu Ngokhululuka, Ngwachisoni." ²

² Kungonena chabe pakamwa kuti ndikumkonda Mtumiki Muhammad (SAW) pomwe zochita zako nzosalingana ndimalangizo a Mtumiki Muhammad (SAW), chikondi chotere chilibe phindu lamtundu uliwonse. Ngati Muhammad (SAW) tikumkondadi timumvere ndi Kumuyesa chitsanzo chathu pazochita zathu zonse.
°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°
32. Nena: "Mverani Mulungu ndi Mtumiki (wake)". Koma ngati Akana, (Mulungu Awakhaulitsa). Ndithudi, Mulungu sakonda Anthu osakhulupirira.

33. Ndithudi Mulungu adasankha Adam ndi Nuh ndi banja La Ibrahim ndi banja la Imran pa zolengedwa Zonse (anthu onse).

34. Ana; ena kuchokera Mwa ena pakati pawo. Ndipo Mulungu Ngwakum va, Ngodziwa.³

³ 🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
Ndime iyi ikusonyeza kuti mawere awa ali olumikizana. Ndipo ikusonyeza kuti anthu abwino ambiri amabala anthu abwino. Tero amene akufuna kukwatira asankhe nyumba yabwino yachipembedzo, yamaphunziro ndi yaluso.
°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°
35. (Kumbukirani) pamene adanena Mkazi wa Imran (Mayi wa Mariam (Maria), M'mapemphero ake): "Mbuye wanga! Ndapereka Kwa inu chimene chili m'mimba Mwanga monga "Wakfu" (wotumikira M'kachisi Wanu). Tero landirani Ichi kwa ine. Ndithudi, Inu Ndinu Akumva, Wodziwa. ⁴

⁴ 🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
(Ndime 35-6) Mkazi wa Imran pamene adali ndi pakati, ankaganiza kuti adzabereka mwana wa mwamuna. Ndipo adalonjeza kwa Mulungu kuti mwanayo adzampereka kuti akhale wotumikira ku Msikiti wa Baiti Limakadasi (Yelusalemu), ndi kutinso adzatumikire pazinthu zina zachipembedzo. Ntchito yake idzangokhala yokhayo. Koma mwatsoka adabereka mwana wamkazi ndipo kuti adzakhale mwana wabwino nkutinso adzabereke ana abwino. Adamutcha otumikira Mulungu. Tero mayi Mariam adali mayi wabwino. Ndipo nayenso adabala mwana wabwino yemwe ndi Mneneri Isa (Yesu). Mariam ndi mayi wolemekezeka kwabasi.
°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°
36. Choncho pamene adam'bala adati: "Mbuye wanga! Ndabala wamkazi!" Ndipo Mulungu akudziwa kwambiri Chimene wabereka - "Ndipo Wamwamuna (yemwe ndimayembekezera Kubala) sali ngati wachikazi (amene Ndamubala. Sangathe kutumikira Moyenera mkachisi wanu). Ndipo ine ndamutcha Mariam (Wotumikira Mulungu). Ndipo ndikupempha Chitetezo Chanu Pa iye ndi ana ake kwa Satana wothamangitsidwayo".

37. Choncho Mbuye wake adamulandira, Kulandira kwabwino; namkulitsa, Kukulitsa kwabwino. Adampatsa Zakariya kuti amulere. Nthawi Iliyonse Zakariya akamulowera Mchipinda mwake (mwa Mariam) M'kachisimo, amampeza Ali ndi chakudya. Amati; "I we, Mariam! ukuzipeza kuti izi?" (Iye) amati: "Izi zikuchokera kwa Mulungu. Ndipo Mulungu Amampatsa yemwe wamfuna popanda Chiyembekezo (mwini wakeyo)".¹

38. Pompo Zakariya adapempha Mbuye wake Nati: "Mbuye wanga! Ndipatseni Kuchokera kwa Inu mwana wabwino. Ndithudi, Inu ndinu Akumva pempho!"²

39. Mwadzidzidzi, mngelo adamuitana Uku iye ataimirira akupemphera Mchipinda cha m'kachisi: "Mulungu akukuuza nkhani yabwino (Yakuti ubereka mwana; dzina lake) Yahaya yemwe adzakhala wotsimikizira (Mneneri yemwe adzabadwa) ndi liwu Lochokera kwa Mulungu, (yemwe ndi Mneneri Yesu) amene adzakhalanso wolemekezeka ndi Wolungama ndi mneneri wa mwa anthu abwino.

🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
¹ Bambo Imran, tate wake wa Mariam, adali munthu wamkulu mwaanthu akuluakulu owopa Chauta panthawiyo. Atamubala mwana wakeyu iye adamwalira. Choncho akuluakulu amene adali naye pamodzi, anapikisana pankhani yolera Mariam. Kenako adagwirizana kuti achite mayere. Amene amgwere ndiyemwe alere Mariam. Tero mayerewo adakomera Mneneri Zakariya, mwamuna wa mayi wake wamng'ono wa mariam. Ndipo Mulungu adamsonyeza Zakariya zododometsa zambiri kwa mwanayo. Zina mwazododometsa ndiko kupeza chakudya pamalo pomwe ankakhala mwanayo chomwe chidali chosadziwika kwa anthu kumene chachokera. Ndipo akamufunsa amati Mulungu ndiye wampatsa.
² Mneneri Zakariya ataona zododometsazo, adaganiza kuti nayenso apemphe kuti amninkhe chozizwitsa chobala mwana pomwe adali wokalamba zedi. Nayenso mkazi wake adali chumba. Ndipo adamubaladi mneneri Yahaya (Yohane).

40. (Zakariya) adati: "Mbuye wanga! Ndidzakhala bwanji ndi mwana Pomwe ukalamba wandifikira, Nayenso mkazi wanga nchumba" (Mngelo adati) "Ndimomwemo; Mulungu amachita Chimene wafuna."

22/01/2021

13. "Ndithudi, padapezeka chisonyezo chachikulu Kwa inu m'magulu awiri omwe adakumana (Tsiku lankhondo ya Badri), pomwe gulu Limodzi limamenya (nkhondo) panjira ya Mulungu, pamene linalo lokanira (ndipo gululo) Linkawaona (Asilamu) kukhala ochuluka kawiri Kuposa ilo, poona ndi maso awo. Ndipo Mulungu amamlimbikitsira mphamvu Ndi chipulumutso chake amene wamfuna. Ndithudi, m'zimenezo muli malingaliro (akulu) Kwa eni kupenyetsetsa mwanzeru."

14. Kwakometsedwa kwa anthu kukonda Zilakolako (Zamoyo monga) akazi, ana, Milumilu yachuma cha golide ndi Siliva ndi mahachi oyang'aniridwa Bwino, ziweto, ndi mbewu. Izo ndi zosangalatsa za moyo Wadziko lapansi (zomwe sizilikanthu). Koma kwa Mulungu ndiko kuli Mabwerero abwino.

15. Nena: "Kodi ndikuuzeni zomwe Zili zabwino kuposa zimenezo? Kwa omwe ali olungama, Akapeza kwa Mbuye wawo Minda yomwe pansi Pake ndi patsogolo pake Mitsinje ikuyenda; Adzakhala Mmenemo muyaya ndikulandira Akazi oyeretsedwa ndi chiyanjo Chochokera kwa Mulungu. Ndipo Mulungu akuona Akapolo ake onse.

16. Omwe akunena: "Mbuye wathu! Ndithudi, ife takhulupirira. Choncho tikhululukireni Machimo athu ndikutipewetsa Kuchilango chamoto."

17. Opirira onena zoona, omvera, Opereka chaulere ndi Opempha chikhululuko Nthawi yam'bandakucha.

18. Mulungu (mwini) akuikira umboni kuti: "Palibe wopembedzedwa mwachoonadi koma lye basi." Ndipo akuikiranso umboni (Zomwezi) angelo ndi eni nzeru (kuti lye) Ngokhazikitsa chilungamo. Palibe wina Wopembedzedwa mwachoonadi koma lye. Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.

19. Ndithudi, chipembedzo (choona) kwa Mulungu ndi Chisilamu. Ndipo amene Adapatsidwa Buku (Ayuda ndi Akhrisitu) sadatsutsane koma pambuyo Powabwerera kuzindikira. (Adatsutsana) Chifukwa chadumbo lomwe lidali Pakati pawo. Ndipo amene akukana Zisonyezo za Mulungu, (Mulungu akamulanga pa tsiku lachiweruzo). Ndithu Mulungu Ngwachangu powerengera.

20. Ngati (osakhulupirira) atsutsana nawe, Nena: "Ndayang'anitsa nkhope yanga Kwa Mulungu (ndadzipereka kwa lye) Pamodzi ndi amene anditsata." Ndipo Nena kwa onse adapatsidwa Buku (Ayuda Ndi Akhrisitu) ndi osadziwa kulemba Ndi kuwerenga (Arabu): "Kodi mwagonjera (Kwa Mulungu)?" Ngati agonjera ndiye Kuti aongoka: Koma ngati atembenukira Kumbali, udindo wako ndikufikitsa uthenga Basi. Ndipo Mulungu akuona akapolo ake onse.

21. Ndithudi, amene akutsutsa Zizindikiro za Mulungu ndikupha Aneneri popanda choonadi Ndikuphanso anthu omwe Akulamula (kuchita) zolungama, Auze nkhani ya chilango chopweteka.

22. Iwowo ndi omwe zochita Zawo zaonongeka Padziko lapansi ndi patsiku Lomaliza. Ndipo iwo sadzapeza athandizi.

23. Kodi sukuwaona omwe apatsidwa Gawo la Buku (la Mulungu)? Akuitanidwa ku Buku la Mulungu Kuti liwaweruze pakati pawo; Kenako gulu Una la iwo Likutembenukira kumbali iwo ali onyoza.¹

¹ 🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
Ndimeyi anthu omasulira Qur'an akuti ikufotokoza nkhani za Ayuda pamene adadza kwa Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) mmodzi mwaiwo atachita chiwerewere kuti arrive chilamulo chawochita chiwerewere. Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) anagamula kuti amulase ndi miyala mpaka afe. Koma iwo anakana. Anati; "M'Buku lathu mulibe chilamulo chotere." Ndipo adawauza kuti abwere nalo bukulo. Atabwera nalo anapeza kuti chilamulocho chilipo. Ndipo anawalasa miyala. Zitachitika tero, Ayuda anakwiya.
°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°
24. Zimenezo (kusalabadira malamulo a Mulungu) Nchifukwa chakuti amanena: "Sudzatikhudza Moto koma masiku ochepa basi". Ndipo Zawanyenga pachipembedzo chawo zomwe Adali kupeka (kuti adzakhululukidwa kapena Kulangidwa masiku ochepa okha).

25. Kodi zidzakhala zotani pamene Tidzawasonkhanitsa tsiku lopanda Chikaiko? Ndipo mzimu uliwonse Udzalipidwa mokwanira pa Zomwe udachita. Ndipo iwo Sadzaponderezedwa.

26. Nena "O! Mbuye wanga! Mwini Ufumu wonse. Mumapereka ufumu kwa yemwe mwamfuna. Ndipo Mumachotsa ufumu kwa yemwe Mwamfuna. Mumapereka ulemerero Kwa emwe mwamfuna, ndipo Mumamsambula yemwenso mwamfuna. Ubwino wonse uli m'manja mwanu. Ndithudi, Inu ndinu Wokhoza chirichonse.

27. "(Inu) mumalowetsa usiku muusana (Ndikukhala usana wautali monga m'nyengo Yotentha). Ndipo Mumalowetsa usana muusiku (Nkukhala usiku wautali monga m'nyengo Yachisanu). Mumatulutsa cha moyo M'chakufa; Ndipo mumatulutsa chakufa M'chamoyo. Ndipo mumapatsa Riziki (Chakudya) amene mwamfuna Mopanda chiwerengero." ¹

¹ 🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
M'njere mumatuluka mmera. Ndipo njere imatuluka mummera. Dzira limatuluka m'nkhuku, ndipo nkhuku imatuluka m'dzira. Wosakhulupirira amabereka wokhulupirira. Ndipo wokhulupirira amabereka wosakhulupirira.
°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°
28. Asilamu asapale ubwenzi osakhulupirira Kusiya Asilamu anzawo. Amene Achite zimenezo, sadzakhala ndi Chilichonse pachipembedzo cha Mulungu, kupatula (kupalana Nawo ubwenzi mwachiphamaso) Chifukwa chakudzitchinjiriza kwa iwo. Ndipo Mulungu lye mwini Akukuchenjezani (za chilango chake). Ndipo kobwerera ndi Kwa Mulungu (basi).

29. Nena: "Ngati mubisa zomwe Zili m'zifuwa zanu, kapena Kuzionetsa (poyera), Mulungu Akuzidziwa. lye akudziwa Zonse zakumwamba Ndi zapansi. Ndipo Mulungu Ngokhoza chilichonse."

20/01/2021

1. Alif-Lam-Mim
الم

🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
Ndime makumi asanu ndi atatu 80 zamsurayi zidavumbuluka chifukwa cha nthumwi za Akhrisitu zochokera ku Najirani pamene zidadza kwa Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye). Nthumwizi zinali 60 okwera pa nyama.Mwa iwo mudali anthu khumi ndi anayi omwe adali olemekezeka awo. Ndipo atatu mwa iwo adali akuluakulu awo omwe ndi: Abdul Masihi, yemwe adali mtsogoleri wawo, Al-Ayihamu, yemwe adali mlangizi wawo, Abu Harisa bun Al-Kama, yemwe adali wansembe wawo. Pamene adakumana ndi Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) atatu aja mwa iwo ndiwo adalankhula nati: "Yesu` ndiye Mulungu chifukwa chakuti iye adali kuutsa maliro." Penanso adati: "lye ndi mwana wa Mulungu chifukwa choti inu simukudziwa kuti Mbuye wathu Mulungu ngwamoyo wamuyaya, safa, pomwe adalibe bambo." Natinso: "lye ndi mmodzi mwa atatu chifukwa chakuti Mulungu adati, "tidachita," "tidati." Akadakhala mmodzi akadati "Ndidachita; ndidanena." Mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adati kwaiwo: "Kodi Yesu ngwakufa?" Iwo adati: "Inde." Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adatinso: "Kodi simukudziwa kuti sipangakhale mwana pokhapokhapo atafanana nditate wake?" Iwo adati: "Inde." lye adatinso: "Kodi simukudziwa kuti Mbuye wathu Mulungu ndiYemwe akuimiririra chinthu chilichonse pochisunga ndi kuchipatsa zofuna zake? Kodi Yesu amachita chilichonse mwazimenezi?" Iwo adati: "lyayi" Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adatinso: "Kodi simukudziwa kuti kwa Mulungu palibe chingabisike chakumwamba ndi chapansi? Nanga Yesu amadziwa chilichonse mwazimenezo osati chokhacho chimene wadziwitsidwa?" Iwo adati: "lyayi." Ndipo iye adatinso: "Kodi simukudziwa kuti Mbuye wathu Mulungu sakudya chakudya ndipo sakumwa ndiponso sadzithandiza pomwe Yesu adali kudya ndi kumwa ndipo adali kudzithandiza?" Iwo adati: "Inde." Ndipo Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adati: "Nanga iye angakhale bwanji Mulungu monga momwe mukunenera?" Onse adangoti kakasi. Komabe adapitiriza kumkana Mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye). Choncho Mulungu chifukwa cha iwo adavumbulutsa ndime zam'surayi kuyambira ndime 1 mpaka 80.
_________________________________

2. Mulungu (ndi mmodzi). Palibe winanso Wopembedzedwa mwa choonadi koma lye yekha, Wamoyo Wamuyaya, Woimira Ndi kuteteza chilichonse.
-اللّهُ لا إِلَـهَ إِلاَّ هُوَ الْحَيُّ الْقَيُّومُ

🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
Mulungu ndiyekhayo woti nkumpembedza. Palibe wina wompembedza mwachoonadi koma lye basi. Padziko lonse lapansi ndi kumwamba palibe mwini mphamvu zoposa wogonjetsa chilichonse koma lye yekha basi. lye ndi Yemwe amadzetsa zabwino ndikubweretsa zoipa, osati wina aliyense. lye Ngwamoyo Wamuyaya, moyo wopanda chiyambi ndiponso wopanda malekezero. lye Ngwachikhalire kuyendetsa zinthu zazolengedwa zake. Thambo ndi nthaka adazikhazikitsa. Apa nkuti Mneneri Yesu asanamlenge. Choncho, Yesu sali Mulungu koma ndimmodzi wa aneneri.
°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°
3. Wakuvumbulutsira Buku Mwachoonadi, lomwe Likutsimikizira zomwe Zidalipo patsogolo pake. Ndipo adavumbulutsa Taurat ndi Injili - (Chipangano Chatsopano).

4. Kale, kuti (mabukuwo) akhale chotsogolera Anthu. Ndipo adavumbulutsa (Qur'an) Cholekanitsa pakati pa choonadi ndi chonama.² Ndithudi, aja amene sadakhulupirire zizindikiro za Mulungu, adzakhala ndi chilango chaukali. Ndipo Mulungu ngwamphamvu Zoposa, wobwezera (Chilango mwaukali).

² 🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
Tanthauzo la ndime iyi nkuti yakuvumbulukira iwe Muhammad (SAW) iyi Qur'an mwachoonadi popanda chipeneko kuti idachokera kwa Mulungu. Yatsika kupyolera mkudziwa Kwake itsimikizire zimene ztdali m'mabuku apatsogolo pake. Ndipo pazimenezi angelo ndimboni.
°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°
5. Ndithudi, kwa Mulungu Sikungabisike chilichonse Chapansi ngakhale chakumwamba.

6. lye ndi Yemwe amakulinganizani Muli m'mimba mmaonekedwe Anu mmene akufunira. Palibe wopembezedwa Mwachoonadi koma lye; Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.

7. lye ndiYemwe wakuvumbulutsira Buku (ili la Qur'an), lomwe mkati Mwake muli ndime zomveka zomwe Ndi maziko a Bukuli. Ndipo Zilipo zina zokuluwika. Koma amene M'mitima mwawo muli kusokera, Akutsata zomwe zili zokuluwika Ndi cholinga chofuna kusokoneza Anthu, ndikufuna kudziwa tanthauzo Lake lenileni, Palibe amene akudziwa Tanthauzo lake lenileni koma Mulungu basi. Koma Amene azama pamaphunziro, amanena: "Tawakhulupirira (ma aya amenewa). Onse Ngochokera kwa Mbuye wathu," Ndipo palibe angakumbukire Koma eni nzeru basi.

8. (Anzeruwo amanena): " O! Mbuye wathu! Musaikhotetse mitima Yathu pambuyo potiongola. Tipatseni chifundo chochokera Kwa Inu. Ndithudi, Inu Ndinu wopatsa kwambiri.

9. O! Mbuye wathu! Inu ndinu Wosonkhanitsa anthu patsiku Lopanda chikaiko, Ndithudi, Mulungu Saswa lonjezo. I)

10. Ndithu, amene sadakhulupirire, Chuma chawo sichidzawathandiza Chilichonse ngakhalenso Ana awo, kuchilango cha Mulungu. Ndipo iwo Ndi nkhuni zakumoto.

11. (Khalidwe la awa osakhulupirira, amumbadwo Wako iwe Mneneri Muhammad {SAW}, liri) Ngati khalidwe la anthu a Farawo ndi amene Adalipo pambuyo pawo. (Iwo) adatsutsa Zisonyezo zathu. Choncho, Mulungu Adawakhaulitsa chifukwa cha machimo awo. Ndipo Mulungu Ngolanga mwaukali.

12. Auze amene sadakhulupirire: "Posachedwapa mugonjetsedwa Ndikusonkhanitsidwa ndikuponyedwa Kumoto. Taonani kuipa kwa Malo wokhazikika." ¹

¹ 🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
Mawu adalandiridwa kuchokera kwa Said bun Jubeir omwe iye adawalandiranso kuchokera kwa Ikirama pomwe nayenso Ikirama adawalandira kuchokera kwa Ibinu Abbas (Mulungu asangalale nawo onse). lye adati: "Ndithudi, Mtumikl (madalitso ndi mtendere zikhale naye) pamene adagonjetsa Akuraishi pankhondo ya Badri nabwerera ku Madina adawasonkhanitsa Ayuda mumsika wa Bani Kainuka nawachenjeza kuti chingawapeze chomwe chidawapeza Akuraishi. Iwo adati: "Usanyengedwe ndizimenezo. Ndithudi, iwe unakumana ndi mbuli za anthu zomwe sizidziwa kamenyedwe kankhondo. Ndipo nchifukwa chake wawagonjetsa. Ukadamenyana ndi ife ukadadziwa kuti ife ndife anthu." Pachifukwa ichi idavumbulutsidwa aya (ndime) yakuti: "Nena (kwa iwo iwe Muhammad {SAW}): "Inu Ayuda mugonjetsedwa posachedwapa pompano padziko lapansi. Chuma chanu ndi ana anu zisakunyengeni. Kupambana sikuli pachifukwa chakuchuluka kwanu, koma kuli m'manja mwa Mulungu Woyera." Mawuwa adatsimikizika powapha a Bani Nazwiri ndi kugonjetsa mzinda wa Khaibar.
°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°

30/12/2020

M'dzina la Mulungu, Wachifundo Chambiri, Wachisoni

1. Alif-Lam-Mim
الم

🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
Ndime makumi asanu ndi atatu 80 zamsurayi zidavumbuluka chifukwa cha nthumwi za Akhrisitu zochokera ku Najirani pamene zidadza kwa Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye). Nthumwizi zinali 60 okwera pa nyama.Mwa iwo mudali anthu khumi ndi anayi omwe adali olemekezeka awo. Ndipo atatu mwa iwo adali akuluakulu awo omwe ndi: Abdul Masihi, yemwe adali mtsogoleri wawo, Al-Ayihamu, yemwe adali mlangizi wawo, Abu Harisa bun Al-Kama, yemwe adali wansembe wawo. Pamene adakumana ndi Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) atatu aja mwa iwo ndiwo adalankhula nati: "Yesu` ndiye Mulungu chifukwa chakuti iye adali kuutsa maliro." Penanso adati: "lye ndi mwana wa Mulungu chifukwa choti inu simukudziwa kuti Mbuye wathu Mulungu ngwamoyo wamuyaya, safa, pomwe adalibe bambo." Natinso: "lye ndi mmodzi mwa atatu chifukwa chakuti Mulungu adati, "tidachita," "tidati." Akadakhala mmodzi akadati "Ndidachita; ndidanena." Mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adati kwaiwo: "Kodi Yesu ngwakufa?" Iwo adati: "Inde." Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adatinso: "Kodi simukudziwa kuti sipangakhale mwana pokhapokhapo atafanana nditate wake?" Iwo adati: "Inde." lye adatinso: "Kodi simukudziwa kuti Mbuye wathu Mulungu ndiYemwe akuimiririra chinthu chilichonse pochisunga ndi kuchipatsa zofuna zake? Kodi Yesu amachita chilichonse mwazimenezi?" Iwo adati: "lyayi" Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adatinso: "Kodi simukudziwa kuti kwa Mulungu palibe chingabisike chakumwamba ndi chapansi? Nanga Yesu amadziwa chilichonse mwazimenezo osati chokhacho chimene wadziwitsidwa?" Iwo adati: "lyayi." Ndipo iye adatinso: "Kodi simukudziwa kuti Mbuye wathu Mulungu sakudya chakudya ndipo sakumwa ndiponso sadzithandiza pomwe Yesu adali kudya ndi kumwa ndipo adali kudzithandiza?" Iwo adati: "Inde." Ndipo Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adati: "Nanga iye angakhale bwanji Mulungu monga momwe mukunenera?" Onse adangoti kakasi. Komabe adapitiriza kumkana Mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye). Choncho Mulungu chifukwa cha iwo adavumbulutsa ndime zam'surayi kuyambira ndime 1 mpaka 80.
_________________________________

2. Mulungu (ndi mmodzi). Palibe winanso Wopembedzedwa mwa choonadi koma lye yekha, Wamoyo Wamuyaya, Woimira Ndi kuteteza chilichonse.
-اللّهُ لا إِلَـهَ إِلاَّ هُوَ الْحَيُّ الْقَيُّومُ

🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
Mulungu ndiyekhayo woti nkumpembedza. Palibe wina wompembedza mwachoonadi koma lye basi. Padziko lonse lapansi ndi kumwamba palibe mwini mphamvu zoposa wogonjetsa chilichonse koma lye yekha basi. lye ndi Yemwe amadzetsa zabwino ndikubweretsa zoipa, osati wina aliyense. lye Ngwamoyo Wamuyaya, moyo wopanda chiyambi ndiponso wopanda malekezero. lye Ngwachikhalire kuyendetsa zinthu zazolengedwa zake. Thambo ndi nthaka adazikhazikitsa. Apa nkuti Mneneri Yesu asanamlenge. Choncho, Yesu sali Mulungu koma ndimmodzi wa aneneri.
°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°°
3. Wakuvumbulutsira Buku Mwachoonadi, lomwe Likutsimikizira zomwe Zidalipo patsogolo pake. Ndipo adavumbulutsa Taurat ndi Injili - (Chipangano Chatsopano).

27/12/2020

282. E inu amene
mwakhulupirira! Mukamakongozana Ngongole kwa
nyengo yodziwika Ilembeni. Ndipo
mlembi pakati Panu alembe mwachilungamo; Ndipo mlembi asakane kulemba Monga momwe Mulungu Wamphunzitsira;
choncho alembe. Ndipo alakatule (mawu olembedwawo Ndi wokongolayo) yemwe ngongole ili paiye. Nayenso aope Mulungu, Mbuye wake, ndipo asapungule Chilichonse M'menemo (m'ngongole). Ndipo ngati wokongola ndiozelezeka kapena Wofooka, kapena iye mwini sangathe Kulembetsa (Momveka),
choncho amulembetsere Myang'aniri (Wakili) wake (yemwe Akuyang'anira zinthu zake) mwachilungamo. Ndipo funiraponi mboni ziwiri Zochokera mwa anthu anu aamuna (Asilamu). Koma ngati amuna awiri Palibe, choncho apezeke Mwamuna mmodzi ndi akazi awiri (Kuti aikire umboniwo), amene mumavomereza Kukhala mboni kuti ngati mmodzi mwaiwo (Akazi awiriwo) angaiwale Mmodzi wawo akumbutse winayo. Ndipo Mboni zisakane zikaitanidwa. Ndiponso Musanyozere kulemba (ngongoleyo) yaing'ono Kapena yaikulu mpaka nyengo yake. Zimenezo (Kulembako) ndibwino kwa Mulungu, ndipo Ncholungama zedi kumbali yaumboni, ndiponso Nchothandiza kuti musakhale ndi chipeneko. Koma akakhala malonda omwe ali Pompo omwe mukupatsana pakati panu (tsintho) Sikulakwa kwainu kusalemba. Koma Funani mboni pamene mukugulitsana. Komatu Asavutitsidwe mlembi ndiponso mboni. Ngati Mutachita zimenezo (zoletsedwazo) kumeneko Ndiko kutuluka m'chilamulo cha
Mulungu wanu, ndipo opani Mulungu, Mulungu akukuphunzitsani. Ndipo Mulungu Ngodziwa chilichonse.

🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
Apa akuwalimbikitsa anthu kuti azilemba akamakongozana zinthu kuti pasakhale mkangano ndikukanirana kuti sanakongozane. Ngakhale ngongoleyo ikhale yochepa pafunika ndithu kulemba. Ndipo polembetsa ngongoleyo wokongolayo ndiye adzinena mawu olembedwawo poopa kuti akayankhula wokongoza akhoza kuonjeza mawu ndipo wokongola nkuchita manyazi kumbweza pakuti mkono wopempha ngwapansi pomwe wopereka ngwapamwamba. Ndipo pamene wolemba akuuzidwa kuti asawakanire kuwalembera osadziwa kulemba, akutanthauza kuti anthu azithandizana pakati pawo. Ndipo olemba akuwalangizanso kuti alembe zokhazo zomwe akuuzidwa ndipo afunirepo mboni zotsimikiza kuti alembadi. Ndipo mbonizo zisainire pamenepo. Oikira umboni afunika kukhala amuna awiri a Chisilamu. Ngati palibe amuna awiriwo, mmalo mwa mwamuna mmodzi zilowe mboni ziwiri za chikazi chifukwa chikumbumtima chaakazi nchochepa poyerekeza ndi chaamuna. Ndipo anthu akuwauzanso kuti akawapempha kuti aikire umboni pachinthu asakane. Kuikira umboni ndi ntchito yabwino yotsimikizira choona ndi kukana chonama. Koma pamalonda ogulitsana dzanja ndi dzanja
sipafunika kulemba koma pamangofunika mboni basi. Ndipo pomwe kwanenedwa kuti "Asavutitsidwe olembawo ndi oikira umboniwo" akusonyeza
kuti ngati ntchito yolembayo ndi kuikira umboniwo nzotenga nthawi yaitali kotero kuti olembawo ndi mbonizo iwachedwetsera ntchito zawo zomwe amapezera zowathandiza pamoyo wawo, ayenera kuwalipira.
°°°° °°°° °°°° °°°° °°° °°°° °°°°
283. Ngati muli paulendo, ndipo Simudapeze mlembi, choncho (Wokongoza) apatsidwe chikole (Pinyolo) m'manja mwake. Ngati
wina Wasungitsa mmodzi wainu chinthu (Omuyesa wokhulupirika) choncho Amene wayesedwa wokhulupirikayo Abweze
chinthucho kwamwini wake, Ndipo aope Mulungu, Mbuye wake. Ndipo musabise umboni (Ngakhale uli wokuipirani). Ndipo
Amene abise ndiye kuti mumtima Mwake mwalowa utchimo; ndipo Mulungu akudziwa zonse zimene mukuchita.

🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
Apa akunena kuti ngati anthu ali pamalo pomwe palibe wodziwa kulemba
ndipo akukongozana, wokongozedwayo apereke chikole kwa wokongoza kuti
achisunge wokongozayo. Ndipo adzabwezera akadzabweza ngongoleyo. Ngati atalephera kubweza ngongoleyo chikolecho chigulitsidwe ndi muweruzi nkumpatsa wokongozayo ndalama zolingana nzomwe adamkongoza.
Zotsalira pachinthu chogulitsidwacho azipereke kwa mwini chikolecho. Uwu ndiwo ubwino wachikole pa Malamulo a Chisilamu. Akalephera kubweza ngongoleyo chinthucho chimagulitsidwa ndi Boma ndikumpatsa mwini ngongoleyo choyenerana naye pomwe chotsaliracho amachipereka kwa
mwini wake.

Kwa amene wagwirizira chikolecho saloledwa kuchita nacho chilichonse. Ngati akuchita nacho ntchito nkumachidyerera ndiye kuti akuchita machitidwe akatapira omwe ali oletsedwa. Koma chinthucho angochisunga.

284. Zonse zakumwamba ndi Zapansi nza Mulungu. Kaya Muonetsera poyera zomwe Zili m'mitima mwanu kapena
Kuzibisa, Mulungu adzakuchitirani Nazo chiwerengero. Kenako Adzakhululukira amene wamfuna (atalapa). Ndipo adzamlanga amene Wamfuna (akapanda kulapa). Ndipo Mulungu Ngokhoza chilichonse.

285. Mtumiki wakhulupirira zimene zavumbulutsidwa Kwa iye kuchokera kwa Mbuye wake. Naonso Asilamu (akhulupirira). Onse Akhulupirira Mulungu, Angelo Ake, mabuku Ake ndi atumiki Ake. (I wo pamodzi ndi Mtumiki wawoyo akunena kuti): "Sitingalekanitse aliyense pakati pa atumiki Ake. (Onse tikuwakhulupirira)." Ndipo akunena: "Tamva ndiponso tamvera. (choncho Tikukupemphani) chikhululuko chanu, E! Mbuye Wathu! Ndipo kwa Inu nkobwerera."

286. Mulungu sakakamiza mzimu Uliwonse koma chimene chili cholingana Ndi kukhoza kwake. (Ndipo phindu la) Zimene mzimuwo udapeza ndilake Ndiponso kuluza kwazomwe Udapeza nkwake. (Asilamuwo amanena) "O! Mbuye wathu! Musatilange tikaiwala Kapena tikalakwitsa, O, Mbuye wathu! Musatisenzetse mtolo (wamalamulo) monga munawasenzetsera amene adalipo Patsogolo pathu. O! Mbuye Wathu Musatisenzetse chimene Sitingachithe. Tifafanizireni, tikhululukireni Machimo athu, ndiponso tichitireni chifundo. Inu Ndinu mtetezi wathu. Choncho Tithangateni ku anthu osakhulupirira."

🅝🅓🅔🅜🅐🅝🅖🅐
(Ndime 285-6) Ndime ziwirizi zili ndiubwino ndi madalitso ambiri monga momwe ilili ndime ya Ayatu Kursii yanambala 255 m'sura yomweyi. Akutilangiza kuziwerenga ndimezi m'malo monse momwe Ayatu Kursii imawerengedwa. Chimodzi mwazimenezo ndikuti iwo amavomereza atumiki
onse a Mulungu amene adadza patsogolo pa Mneneri Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye). Qur'an yonse ikuphunzitsa Asilamu kuti asasiyanitse pakati pa aneneri. Koma awavomereze onse ndi kuwakhulupirira amene adadza patsogolo pa Mtumiki Muhammad (SAW). Mtumiki Muhammad (SAW) ndiye womaliza mwa Aneneriwo. Ndipo amadziwika ndi dzina lakuti "Khatama nNabiyyina" "Womaliza mwa Aneneri." Ndipo amene sakhulupirira kuti Muhammad (SAW) ngomaliza mwa aneneri nakhulupirira munthu wamba yemwe akungodzinamiza kuti iye ndi mneneri, monga momwe chikhulupiriro cha Akadiyani chilili ndiye kuti iyeyo watuluka m'Chisilamu ndipo
ndi munthu wakunja.

Asilamu sakana mneneri aliyense mwa Aneneri omwe adalipo Mtumiki
Muhammad (SAW) asanadze. Koma iwo amakhulupirira kuti malamulo akayendetsedwe kazipembedzo zawo kadafafanizidwa chifukwa chakudza
kwa mtumiki Muhammad (SAW). Nyengo ino ndinyengo yotsatira mtumiki
Muhammad (SAW) pazochitachita. Koma pazinthu zokhudza chikhulupiriro,
Aneneri onse adadza ndi lamulo limodzi monga momwe Mulungu
akufotokozera m'ndime ya 13, Surat Shura.

Ndipo m'ndime zimenezi za 285 ndi 286 zikuphunzitsanso miyambo yaChisilamu ndi mapemphero (maduwa) momwe tingampemphere Mulungu. Ndimezi zikufotokoza za chisomo cha Mulungu chomwe chili pa ife anthu Ake kuti Mulungu sakakamiza koma chimene angathe kuchichita akapolo Ake.
Ndiponso sawalanga ngati atachita zinthu molakwitsa kapena moiwala. Ndime ziwirizi zikusonyeza makhalidwe Asilamu ndi zinthu zawo zimene amazikhulupirira

Apa tsopano tamaliza Suratul Baqarah
Alhamdulillah timupemphe Allah kuti atilandile ntchito yathu yolemekezekayi ndikuyipanga kukhala yoyeletsedwa
AAMEEN

Address

Mponda
ABDULLAHISSAHWITNESS

Opening Hours

Monday 05:30 - 22:00
Tuesday 17:00 - 23:25
Wednesday 05:15 - 23:10
Thursday 05:05 - 22:55
Friday 05:15 - 22:30
Saturday 04:10 - 22:45
Sunday 04:00 - 23:00

Telephone

0731930662

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Miftaahul Jannah kiyi wa ku Jannah posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share

Category