04/08/2026
Linali tsiku la chisoni kwambiri pamene thupi la malemu Traditional Authority ( TA) Mponda, limalowa mmanda lero lachiwiri ku likulu kwawo la Kanyenje.
Malemu TA Mponda anamwalira loweruka kuchipatala cha boma cha Mchinji atadwala kanthawi kochepa.
Mkulu oyang'anira mafumu ku unduna wa maboma aang'ono a Charles Makanga anali nawo pa mwambo woyika mmanda malemu mfumuyi ndipo anati malemuwa anali odziwa kuthetsa mikangano komanso amadziwa zambiri za zitukuko.
A Makanga anapempha a ku banja kuti apewe mikangano pamene akusankha mlowammalo wa malemuwa.
A ku banja asankha a Alines Makaniko kuti alowe mmalo mwa mfumu yatisiyayi.
Anthu ochuluka kuphatikiza mafumu a chiChewa, akuluakulu a khonsolo komanso anthu a kuderali anaperekeza malemu wa.
Malemu TA Mponda asiya mkazi ndi ana asanu ndi anayi.