28/05/2026
Khonsolo ya Mchinji lero ikukhazikitsa lamulo lomwe mtsogoleri wa dziko lino anakhazikitsa losamalira malo ndi ukhondo mmalo omwe akukhala komanso kuchitira malonda.
Mwambowu ukuchitikira ku Kapiri komwe khonsoloyi motsogozedwa ndi bwanankubwa Reinghard Chavula, akusesa mu msika komanso malo ozungulira Trading Centre yi.
Mfumu yaikulu Dambe, wapampando wa khonsolo a Kennedy Chipanga, wamkulu wa polisi a Dr David Kumwenda, akuluakulu a za umoyo, ochita malonda, akuluakulu a mabungwe omwe si aboma, akulu akulu a banki ya Centenary, ogwira ntchito mu boma komanso achinyamata anatenga nawo gawo.
Prof. Arthur Peter Mutharika, anayika lamulo loti malo onse aboma, okwerera mabasi, misika, ndi malo ogwirira ntchito akhale ndi zida zothandizira ukhondo. Cholinga cha lamuloli ndi kuteteza anthu ku matenda monga kolera.
Mwachidule, lamulo li likuti malo aboma ndi misika, malo okwerera mabasi, malo oyima galimoto (car parks), ndi malo ena onse okhala anthu ambiri ayenera kukhala ndi malo abwino otayira zinyalala komanso malo ogwirira ntchito ndi masukulu aboma ndi a private komanso malo ogwirira ntchito ayenera kukhala ndi zida zothandizira ukhondo ndi zotayira zinyalala.
Ma khonsolo ndiponso ma bungwe azaumoyo ayenera kuonetsetsa kuti lamuloli likuyenda.