31/05/2026
BUNGWE LA LET'S BUILD LIPEREKA MA KALASIRUMU BULOKO KHUMI NDI ATATU KU BOMA
Pachiweru, bungwe la Let's Build Foundation - Malawi lapereka ma kalasirumu buloko khumi ndi atatu ku unduna wa zamaphunziro, omwe amangidwa mma sekondale sukulu oyendera (CDSS) asanu ndi awiri m'boma la Dowa.
Mabulokowa amangidwa mma CDSS awa; Kawangi, Nalunga, Simbi, Chimwetsero, Chakhadza, Mdika komanso Tchale.
Nduna yoona zamaphunziro a Bright Msaka, SC, ndi amene analandira makalasirumu bulokowa mmalo mwa boma, pa mwambo omwe unachitikira pa Simbi CDSS mdera la mfumu yaikulu Dzoole.
Iwo athokoza bungweli ponena kuti izi zithandiza kutukula maphunziro m'boma la Dowa. A Msaka atsindikanso kuti boma ndilozipereka kutukula maphunziro, ndipo lionesetsa kuti mmasukulu a sekondale onse muli zipangizo zoyenera zokwanira.
Mkulu wa bungwe la Let's Build Foundation - Malawi mayi Ruth Kamwendo anati ndi cholinga chawo kuthandizira boma kuti ophunzira aliyense athe kukhala ndi kalasi yophunziliramo, ndi cholinga choti maphunziro afikire kwa mwana wina aliyense.
Mabulokowa ndiokhala ndi makalasirumu awiri iliyonse, komanso akudza ndi ma desiki makumi asanu (50) mu kalasi iliyonse.
Bungweli laperekanso zimbuzi khumi ndi zinayi mmasukulu wa, zomwe ndizofikirika kwa ana a ulumali, komanso zokhala ndi zipinda zosinthira za atsikana.
"Tikulengezanso kuti timanganso ma buloko ena ngati amenewa, awiriawiri pa sukulu za Mbalame, Chibanzi komanso Kaungwe," anatero a Kamwendo.
Wachiwiri kwa wapampando wa khonsolo ya Dowa khansala Lenard Kafumbula wapempha ophunzira kuti alimbikire maphunziro awo.